1Wokonda mwambo akonda kudziwa;
koma wakuda chidzudzulo apulukira.
2Yehova akomera mtima munthu wabwino;
koma munthu wa ziwembu amtsutsa.
3Munthu sadzakhazikika ndi udyo,
muzu wa olungama sudzasunthidwa.
4 1Ako. 11.7 Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wake;
koma wochititsa manyazi akunga chovunditsa mafupa a mwamunayo.
5Maganizo a olungama ndi chiweruzo;
koma uphungu wa oipa unyenga.
6Mau a oipa abisalira mwazi;
koma m'kamwa mwa olungama muwalanditsa.
7 Mat. 7.24-27 Oipa amagwa kuli zii;
koma banja la olungama limaimabe.
8 1Sam. 25.17 Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yake;
koma wokhota mtima adzanyozedwa.
9Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,
aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.
10 Deut. 25.4 Wolungama asamalira moyo wa choweta chake;
koma chifundo cha oipa ndi nkhanza.
11 Gen. 3.19 Zakudya zikwanira wolima minda yake;
koma wotsata anthu opanda pake asowa nzeru.
12Woipa akhumba chokodwa ndi amphulupulu;
koma muzu wa olungama umabala zipatso.
13M'kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;
koma wolungama amatuluka m'mavuto.
14 Yes. 3.10-11 Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwake;
zochita za manja ake zidzabwezedwa kwa iye.
15 Luk. 18.11 Njira ya chitsiru njolungama pamaso pakepake;
koma wanzeru amamvera uphungu.
16Mkwiyo wa chitsiru udziwika posachedwa;
koma wanzeru amabisa manyazi.
17Wolankhula ntheradi aonetsa chilungamo;
koma mboni yonama imanyenga.
18 Mas. 59.7 Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga;
koma lilime la anzeru lilamitsa.
19 Mas. 52.4-5 Mlomo wa ntheradi ukhazikika nthawi zonse;
koma lilime lonama likhala kamphindi.
20Chinyengo chili m'mitima ya oganizira zoipa;
koma aphungu a mtendere amakondwa.
21Palibe vuto lidzagwera wolungama;
koma amphulupulu adzadzazidwa ndi zoipa.
22 Chiv. 22.15 Milomo yonama inyansa Yehova;
koma ochita ntheradi amsekeretsa.
23Munthu wanzeru abisa zomwe adziwa;
koma mtima wa opusa ulalikira utsiru.
24Dzanja la akhama lidzalamulira;
koma waulesi adzakhala ngati kapolo.
25 Yes. 50.4 Nkhawa iweramitsa mtima wa munthu;
koma mau abwino aukondweretsa.
26Wolungama atsogolera mnzake;
koma njira ya oipa iwasokeretsa.
27Waulesi samaotcha nyama yake anaigwira;
koma wolungama amalandira chuma chopambana cha anthu.
28M'khwalala la chilungamo muli moyo;
m'njira ya mayendedwe ake mulibe imfa.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.