MASALIMO 143 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Davide apempha Mulungu amlanditse msanga kwa adani akeSalimo la Davide.

1 1Yoh. 1.9 Imvani pemphero langa, Yehova; nditcherere khutu kupemba kwanga;

ndiyankheni mwa chikhulupiriko chanu, mwa chilungamo chanu.

2 Aro. 3.20 Ndipo musaitane mlandu wa mtumiki wanu;

pakuti pamaso panu sipadzakhala wolungama wamoyo mmodzi yense.

3Pakuti mdani alondola moyo wanga;

apondereza pansi moyo wanga;

andikhalitsa mumdima monga iwo adafa kale lomwe.

4Potero mzimu wanga wakomoka mwa ine;

mtima wanga utenga nkhawa m'kati mwanga.

5 Mas. 77.5, 10-11 Ndikumbukira masiku a kale lomwe;

zija mudazichita ndilingirirapo;

ndikamba pandekha za ntchito ya manja anu.

6 Mas. 42.2; 88.9 Nditambalitsira manja anga kwa Inu:

Moyo wanga ulira Inu monga dziko lolira mvula.

7Fulumirani ndiyankheni, Yehova; mzimu wanga ukutha.

Musandibisire nkhope yanu;

ndingafanane nao akutsikira kudzenje.

8 Mas. 46.5; 90.14 Mundimvetse chifundo chanu mamawa;

popeza ndikhulupirira Inu:

Mundidziwitse njira ndiyendemo;

popeza ndikweza moyo wanga kwa Inu.

9Mundilanditse kwa adani anga, Yehova;

ndibisala mwa Inu.

10 Mas. 25.4-5 Mundiphunzitse chokonda Inu; popeza Inu ndinu Mulungu wanga;

Mzimu wanu ndi wokoma; munditsogolere kuchidikha.

11Mundipatse moyo, Yehova, chifukwa cha dzina lanu;

mwa chilungamo chanu mutulutse moyo wanga m'sautso.

12Ndipo mwa chifundo chanu mundidulire adani anga,

ndipo muononge onse akusautsa moyo wanga;

pakuti ine ndine mtumiki wanu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help