DEUTERONOMO Mau Oyamba - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Mau OyambaBukuli likutchedwa Deuteronomo, ndiye kuti “Kubwereza”, chifukwa likulongosola kachiwiri zina ndi zina zimene zidakambidwa kale m'mabuku ena aja. Bukuli likulongosola za malangizo osiyanasiyana amene Mose adapereka kwa ana a Israele pamene anali m'dziko la Mowabu, ali pafupi kulowa m'dziko lamalonjezano la Kanani.Phunziro lalikulu lopezeka m'bukuli ndi lakuti Yehova apulumutsa Aisraele ndi kuwadalitsa chifukwa amawakonda kwambiri. Motero iwonso ayenera kumakumbukira zimenezi ndi kumkonda Iyeyo potsata malamulo ake, kuti akhale ndi moyo ndi kulandirabe madalitso ena pa moyo wao ukudzawu. Mau odziwika kwambiri apezeka pa 6.4-6: “ndipo muzikonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, ndi mphamvu yanu yonse.” Paja Yesu adati, pa malamulo onse, lamulo lalikulu ndi lomweli.Za mkatimuMalangizo oyamba a Mose 1.1—4.49

Malangizo achiwiri a Mose 5.1—26.19

a. Za Malamulo Khumi 5.1—10.22

b. Mose aperekanso malamulo ena ndi malangizo 11.1—26.19

Machenjezo asanalowe m'dziko la malonjezano 27.1—28.68

Yehova achita chipangano ndi anthu ake 29.1—30.20

Malangizo otsiriza a Mose 31.1—34.12

a. Mose asankha Yoswa kuti adzalowe m'malo mwake 31.1—33.29

b. Imfa ya Mose 34.1-12

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help