MASALIMO 42 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Mtima wolira kuyanjana ndi Mulungu mu KachisiKwa Mkulu wa Nyimbo. Chilangizo cha kwa ana a Kora.

1 Yow. 1.20 Monga nswala ipuma wefuwefu kukhumba mitsinje;

motero moyo wanga upuma wefuwefu kukhumba Inu, Mulungu.

2 Mas. 63.1; Yoh. 7.37 Moyo wanga uli ndi ludzu la kwa Mulungu,

la kwa Mulungu wamoyo.

Ndikadze liti kuoneka pamaso pa Mulungu?

3 Mas. 79.10; 80.5 Misozi yanga yakhala ngati chakudya changa,

usana ndi usiku;

pakunena iwo kwa ine dzuwa lonse,

Mulungu wako ali kuti?

4 Mas. 62.8; Yes. 30.29 Ndidzikumbukira izi ndipo nditsanulira moyo wanga m'kati mwa ine,

pakuti ndinkapita ndi unyinji wa anthu,

ndinawatsogolera kunyumba ya Mulungu,

ndi mau akuimbitsa ndi kuyamika,

ndi unyinji wakusunga dzuwa lokondwera.

5 Mas. 43.5 Udziweramiranji moyo wanga iwe?

Ndi kuzingwa m'kati mwanga?

Yembekeza Mulungu, pakuti ndidzamyamikanso

chifukwa cha chipulumutso cha nkhope yake.

6Mulungu wanga, moyo wanga

udziweramira m'kati mwanga;

chifukwa chake ndikumbukira Inu m'dziko la Yordani,

ndi mu Aheremoni, m'kaphiri ka Mizara.

7 Yon. 2.3 Madzi akuya aitanizana ndi madzi akuya,

pa mkokomo wa matiti anu;

mafunde onse a nyondonyondo anandimiza ine.

8 Mas. 77.6; Mac. 16.25 Koma usana Yehova adzalamulira chifundo chake,

ndipo usiku nyimbo yake idzakhala ndi ine.

Inde pemphero la kwa Mulungu wa moyo wanga.

9 Mas. 43.2 Ndidzati kwa Mulungu, thanthwe langa,

mwandiiwala chifukwa ninji?

Ndimayenderanji wakulira

chifukwa cha kundipsinja mdaniyo?

10 Mas. 42.3 Adani anga andinyoza ndi kundithyola mafupa anga;

pakunena ndine dzuwa lonse,

Mulungu wako ali kuti?

11 Mas. 42.5 Udziweramiranji moyo wanga iwe?

Ndi kuzingwa m'kati mwanga?

Yembekeza Mulungu; pakuti ndidzamlemekeza tsopanonso,

ndiye chipulumutso cha nkhope yanga ndi Mulungu wanga.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help