MASALIMO 114 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Alemekeze Mulungu pa chipulumutso chija cha mu Ejipito

1 Eks. 13.3 M'mene Israele anatuluka ku Ejipito,

nyumba ya Yakobo kwa anthu a chinenedwe chachilendo;

2 Eks. 19.6 Yuda anakhala malo ake oyera, Israele ufumu wake.

3 Eks. 14.21; Yos. 3.13, 16 Nyanjayo inaona, nithawa;

Yordani anabwerera m'mbuyo.

4 Mas. 29.6 Mapiri anatumphatumpha ngati nkhosa zamphongo,

timapiri ngati anaankhosa.

5Unathawanji nawe, nyanja iwe?

Unabwereranji m'mbuyo, Yordani iwe?

6 Mas. 29.6 Munatumphatumphiranji ngati nkhosa zamphongo, mapiri inu?

Ngati anaankhosa, zitunda inu?

7Unjenjemere, dziko lapansi iwe, pamaso pa Ambuye,

pamaso pa Mulungu wa Yakobo;

8 Eks. 17.6 amene anasanduliza thanthwe likhale thawale lamadzi,

nsangalabwi ikhale kasupe wamadzi.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help