1Ha! Golide wagugadi; golide woona woposa wasandulika;
miyala ya malo opatulika yakhuthulidwa
pa malekezero a makwalala onse.
2Ana a Ziyoni a mtengo wapatali,
olingana ndi golide woyengetsa,
angoyesedwa ngati mbiya zadothi zozipanga manja a woumba.
3Angakhale ankhandwe amapatsa bere, nayamwitsa ana ao;
koma mwana wamkazi wa anthu a mtundu wanga
wasanduka wankhanza,
ngati nthiwatiwa za m'chipululu.
4
13
sadzagoneranso kuno.
16Mkwiyo wa Yehova unawalekanitsa, sadzawasamaliranso;
iwo sanalemekeze ansembe, sanakomere mtima akulu.
17 2Maf. 24.7 Maso athu athedwa, tikali ndi moyo,
poyembekeza thandizo chabe;
kudikira tinadikira mtundu wosatha kupulumutsa.
18 2Maf. 25.4-5 Amalondola mapazi athu, sitingayende m'makwalala athu;
chitsiriziro chathu chayandikira, masiku athu akwaniridwa;
pakuti chitsiriziro chathu chafikadi.
19 Deut. 28.49 Otilondola anaposa ziombankhanga
za m'mlengalenga m'liwiro lao,
anatithamangitsa pamapiri natilalira m'chipululu.
20 Yer. 52.9 Wodzozedwa wa Yehova,
ndiye mpweya wa m'mphuno mwathu,
anagwidwa m'maenje ao;
amene tinanena kuti,
Tidzakhala m'mthunzi mwake pakati pa amitundu,
21 Oba. 10 kondwera nusangalale, mwana wamkazi wa Edomu,
wokhala m'dziko la Uzi;
chikho chidzapita ngakhale mwa iwenso;
udzaledzera ndi kuvula zako.
22 Mas. 137.7; Yes. 40.2 Mphulupulu yako yatha, mwana wamkazi wa Ziyoni,
Yehova sadzakutenganso ndende;
koma adzazonda mphulupulu yako, mwana wa mkazi wa Edomu,
nadzavumbulutsa zochimwa zako.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.