NYIMBO YA SOLOMONI 8 - Buku Lopatulika Bible 2014

1Mwenzi utakhala ngati mlongo wanga,

woyamwa pa bere la amai!

Ndikadakupeza panja, ndikadakupsompsona;

osandinyoza munthu.

2Ndikadakutsogolera, kukulowetsa m'nyumba ya amai,

kuti andilange mwambo;

ndikadakumwetsa vinyo wokoleretsa,

ndi madzi a makangaza anga.

3Dzanja lamanzere lake akadanditsamiritsa kumutu,

lamanja lake ndi kundifungatira.

4Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu,

muutsiranji, mugalamutsiranji chikondi,

chisanafune mwini.

5

Ngati ndiye chitseko tidzamtsekereza ndi matabwa amikungudza.

10Ndine khoma, mawere anga akunga nsanja zake:

Pamaso pa mnyamatayo ndinafanana ngati wopeza mtendere.

11Solomoni anali ndi munda wamipesa ku Baala-Hamoni;

nabwereka alimi mundawo;

yense ambwezere ndalama chikwi chifukwa cha zipatso zake.

12Koma munda wanga wamipesa,

uli pamaso panga ndiwo wangatu;

nacho chikwicho, Solomoni iwe,

koma olima zipatso zake azilandira mazana awiri.

13Namwaliwe wokhala m'minda,

anzako amvera mau ako:

Nanenanso undimvetse.

14 Chiv. 22.17, 20 Dzifulumira, mnyamatawe wokondedwa wanga,

dzifanane ngati mphoyo pena mwana wa mbawala

pa mapiri a mphoka.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help