MIYAMBO 26 - Buku Lopatulika Bible 2014

1Monga chipale chofewa m'malimwe, ndi mvula m'masika,

momwemo ulemu suyenera chitsiru.

2Monga mpheta ilikuzungulira, ndi namzeze alikuuluka,

momwemo temberero la pachabe silifikira.

3

24Wakuda mnzake amanyenga ndi milomo yake;

koma akundika chinyengo m'kati mwake.

25 Yer. 9.8 Pamene akometsa mau ake usamkhulupirire;

pakuti m'mtima mwake muli zonyansa zisanu ndi ziwiri.

26Angakhale abisa udani wake pochenjera,

koma udyo wake udzavumbulutsidwa posonkhana anthu.

27 Mas. 7.15-16; Mlal. 10.8 Wokumba dzenje adzagwamo,

wogubuduza mwala, udzabweranso pa iye mwini.

28Lilime lonama lida omwewo linawasautsa;

ndipo m'kamwa mosyasyalika mungoononga.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help