MASALIMO 98 - Buku Lopatulika Bible 2014

Alemekeze Mulungu pa chifundo ndi choonadi chaoSalimo.

1 Eks. 15.11-12 Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano;

popeza anachita zodabwitsa:

Dzanja lake lamanja, mkono wake woyera,

zinamchitira chipulumutso.

2 Yes. 52.10 Yehova anawadziwitsira chipulumutso chake;

anaonetsera chilungamo chake pamaso pa amitundu.

3 Mas. 50.3 Anakumbukira chifundo chake ndi chikhulupiriko chake

kunyumba ya Israele;

malekezero onse a dziko lapansi

anaona chipulumutso cha Mulungu wathu.

4 Mas. 95.1; Yes. 44.23 Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi;

kuwitsani ndi kufuulira mokondwera;

inde, imbirani zomlemekeza.

5Muimbireni Yehova zomlemekeza ndi zeze;

ndi zeze ndi mau a salimo.

6Fuulani pamaso pa Mfumu Yehova,

ndi mbetete ndi liu la lipenga.

7 Mas. 96.10-13 Nyanja ifuule ndi kudzala kwake;

dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhalamo;

8mitsinje iombe manja;

mapiri afuule pamodzi mokondwera.

9Pamaso pa Yehova, popeza akudza kudzaweruza dziko lapansi;

adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi chilungamo,

ndipo mitundu ya anthu molunjika.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help