MASALIMO 65 - Buku Lopatulika Bible 2014

Davide alemekeza Mulungu pa madalitso ochulukaKwa Mkulu wa Nyimbo; Salimo la Davide. Nyimbo.

1 Mas. 50.14 M'Ziyoni akulemekezani Inu mwachete, Mulungu,

adzakuchitirani Inu chowindachi.

2 Yes. 66.23 Wakumva pemphero Inu,

zamoyo zonse zidzadza kwa Inu.

3 Mas. 51.2; Yes. 6.7; Aheb. 9.14 Mphulupulu zinandilaka;

koma mudzafafaniza zolakwa zathu.

4 Mas. 33.12; 36.8 Wodala munthuyo mumsankha, ndi kumyandikizitsa,

akhale m'mabwalo anu.

Tidzakhuta nazo zokoma za m'nyumba yanu,

za m'malo oyera a Kachisi wanu.

5 Mas. 22.27 Mudzatiyankha nazo zoopsa m'chilungamo,

Mulungu wa chipulumutso chathu;

ndinu chikhulupiriko cha malekezero onse a dziko lapansi,

ndi cha iwo okhala kutali kunyanja.

6Ndinu amene mukhazikitsa mapiri ndi mphamvu yanu;

pozingidwa nacho chilimbiko.

7 Yes. 17.12-13; Mat. 8.26 Amene atontholetsa kukuntha kwa nyanja,

kukuntha kwa mafunde ake,

ndi phokoso la mitundu ya anthu.

8Ndipo iwo akukhala kumalekezero adzachita mantha

chifukwa cha zizindikiro zanu;

mukondweretsa apo patulukira dzuwa, ndi apo lilowera.

9 Mas. 46.4 Mucheza nalo dziko lapansi, mulithirira,

mulilemeza kwambiri;

mtsinje wa Mulungu udzala nao madzi,

muwameretsera tirigu m'mene munakonzera nthaka.

10Mukhutitsa nthaka yake yolima;

mufafaniza nthumbira zake;

muiolowetsa ndi mvumbi;

mudalitsa mmera wake.

11Muveka chakachi ndi ukoma wanu;

ndipo mabande anu akukha zakucha.

12Akukha pa mabusa a m'chipululu;

ndipo mapiri azingika nacho chimwemwe.

13 Yes. 55.12 Podyetsa mpodzaza ndi zoweta;

ndipo zigwa zakutidwa ndi tirigu;

zifuula mokondwera, inde ziimbira.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help