NYIMBO YA SOLOMONI 1 - Buku Lopatulika Bible 2014

Mkwatibwi anena ndi ana a Yerusalemu za mkwati

1

ngati mahema a Kedara,

ngati nsalu zotchinga za Solomoni.

6Musayang'ane pa ine, pakuti ndada,

pakuti dzuwa landidetsa.

Ana amuna a amai anandikwiyira,

anandisungitsa minda yamipesa;

koma munda wangawanga wamipesa sindinausunga.

7Ndiuze, iwe amene moyo wanga ukukonda,

umaweta kuti gulu lako?

Umaligonetsa kuti pakati pa usana?

Pakuti ndikhalirenji ngati wosochera

pambali pa magulu a anzako?

8Ngati sudziwa, mkaziwe woposa kukongola,

dzituluka kukalondola bande la gululo,

nukawete anaambuzi zako pambali pa mahema a abusa.

Mkwati ndi mkwatibwi akambirana za chikondano chao

9

10

12Pokhala mfumu podyera pake,

narido wanga ananunkhira.

13Wokondedwa wanga mnyamatayo

ali kwa ine ngati thumba la mure,

logona pakati pa mawere anga.

14Wokondedwa wanga ali kwa ine

ngati chipukutu cha maluwa ofiira

m'minda yamipesa ya ku Engedi.

15Taona, wakongolatu, bwenzi langa;

namwaliwe taona, wakongola,

maso ako akunga a nkhunda.

16Taona, wakongolatu, bwenzi langa,

mnyamatawe, inde, wakongoletsa;

pogona pathu mpa msipu.

17Mitanda ya nyumba zathu nja mikungudza,

ndi mapaso athu nga mlombwa.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help