MASALIMO 108 - Buku Lopatulika Bible 2014

Davide aimbira Mulungu womgonjetsera adaniNyimbo. Salimo la Davide.

1Wakhazikika mtima wanga, Mulungu;

ndidzaimba, inde ndidzaimba zolemekeza, ndiko ulemerero wanga.

2Galamukani, chisakasa ndi zeze;

ndidzauka ndekha mamawa.

3Ndidzakuyamikani mwa mitundu ya anthu, Yehova:

ndipo ndidzaimba zakukulemekezani mwa anthu.

4Pakuti chifundo chanu nchachikulu kupitirira kumwamba,

ndi choonadi chanu kufikira mitambo.

5Kwezekani pamwamba pa thambo, Mulungu;

ndi ulemerero wanu pamwamba pa dziko lonse lapansi,

6kuti okondedwa anu alanditsidwe,

pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja ndipo mutivomereze.

7Mulungu analankhula m'chiyero chake; ndidzakondwerera:

ndidzagawa Sekemu; ndidzayesa muyeso chigwa cha Sukoti.

8Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanga;

ndi Efuremu ndiye mphamvu ya mutu wanga;

Yuda ndiye wolamulira wanga.

9Mowabu ndiye mkhate wanga;

pa Edomu ndidzaponya nsapato yanga;

ndidzafuulira Filistiya.

10Adzandifikitsa ndani m'mudzi wa m'linga?

Adzanditsogolera ndani ku Edomu?

11Si ndinu Mulungu, amene mwatitaya

osatuluka nao magulu athu?

12Tithandizeni mumsauko;

pakuti chipulumutso cha munthu ndi chabe.

13Mwa Mulungu tidzachita molimbika mtima:

Ndipo Iye adzapondereza otisautsa.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help