MASALIMO 23 - Buku Lopatulika Bible 2014

Amwai amene Yehova akhala Mbusa waoSalimo la Davide.

1 Yes. 40.11; Yer. 23.3-4; Ezk. 34.11-12, 23; Yoh. 10.11; Afi. 4.19 Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.

2 Ezk. 34.14; Chiv. 7.17 Andigonetsa kubusa lamsipu,

anditsogolera kumadzi odikha.

3Atsitsimutsa moyo wanga;

anditsogolera m'mabande a chilungamo, chifukwa cha dzina lake.

4 Yob. 10.21-22; Mas. 27.1; Yes. 43.2 Inde, ndingakhale ndiyenda m'chigwa cha mthunzi wa imfa,

sindidzaopa choipa; pakuti Inu muli ndi ine;

chibonga chanu ndi ndodo yanu, izi zindisangalatsa ine.

5 Mas. 45.7; 92.10 Mundiyalikira gome pamaso panga m'kuona kwa adani anga;

mwandidzoza mutu wanga mafuta; chikho changa chisefuka.

6Inde ukoma ndi chifundo zidzanditsata

masiku onse a moyo wanga,

ndipo ndidzakhala m'nyumba ya Yehova masiku onse.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help