NYIMBO YA SOLOMONI 6 - Buku Lopatulika Bible 2014

1Bwenzi lako wapita kuti,

mkaziwe woposa kukongola?

Bwenzi lako wapatukira kuti,

tikamfunefune pamodzi nawe?

2Bwenzi langa watsikira kumunda kwake,

kuzitipula za mphoka,

kukadya kumunda kwake, ndi kutchera akakombo.

3

woopsa ngati nkhondo ndi mbendera.

5Undipambutsire maso ako,

pakuti andiopetsa.

Tsitsi lako likunga gulu la mbuzi,

zigona pambali pa Giliyadi.

6Mano ako akunga gulu la nkhosa zazikazi,

zikwera kuchokera kosamba;

yonse ili ndi ana awiri,

palibe imodzi yopoloza.

7Palitsipa pako pakunga phande la khangaza

paseli pa chophimba chako.

8Alipo akazi akulu a mfumu makumi asanu ndi limodzi,

kudza akazi aang'ono makumi asanu ndi atatu,

ndi anamwali osawerengeka.

9Nkhunda yanga, wangwiro wangayu, ndiye mmodzi;

ndiye wobadwa yekha wa amake;

ndiye wosankhika wa wombala.

Ana akazi anamuona, namutcha wodala;

ngakhale akazi akulu a mfumu,

ndi akazi aang'ono namtamanda.

10Nati, Ndaniyo atuluka ngati mbandakucha,

wokongola ngati mwezi,

woyera ngati dzuwa,

woopsa ngati nkhondo ndi mbendera?

11Ndinatsikira kumunda wa mtedza,

kukapenya msipu wa m'chigwa,

kukapenya ngati pamipesa paphuka,

ngati pamakangaza patuwa maluwa.

12Ndisanazindikire, moyo wanga unandiimika

pakati pa magaleta a anthu anga aufulu.

13Anati, Bwera, bwera, Msulamiwe;

bwera, bwera, tiyang'ane pa iwe.

Muyang'aniranji pa Msulami,

ngati pa masewero akuguba?

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help