MASALIMO 70 - Buku Lopatulika Bible 2014

Davide apempha Mulungu amlanditse msangaKwa Mkulu wa Nyimbo; Salimo la Davide, la chikumbutso.

1 Mas. 40.13-17 Fulumirani kundipulumutsa, Mulungu!

Fulumirani kundithandiza, Yehova.

2Achite manyazi, nadodome

amene afuna moyo wanga.

Abwezedwe m'mbuyo, napepulidwe

amene akonda kundichitira choipa.

3Abwerere, kukhale mphotho ya manyazi ao

amene akuti, Hede, hede.

4Asekerere nakondwerere mwa Inu onse akufuna Inu;

nanene kosalekeza iwo akukonda chipulumutso chanu,

abuke Mulungu.

5 Mas. 141.1 Koma ine ndine wozunzika ndi waumphawi;

mundifulumirire, Mulungu.

Inu ndinu mthandizi wanga ndi Mpulumutsi wanga;

musachedwe, Yehova.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help