1
mtundu wa anthu sindinaudziwa udzanditumikira.
44Pakumva m'khutu za ine adzandimvera,
alendo adzandigonjera monyenga.
45Alendo adzafota,
nadzatuluka monjenjemera m'ngaka mwao.
46Yehova ngwa moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;
nakwezeke Mulungu wa chipulumutso changa.
47Ndiye Mulungu amene andibwezerera chilango,
nandigonjetsera mitundu ya anthu.
48Andipulumutsa kwa adani anga.
Inde mundikweza pa iwo akundiukira ine,
mundikwatula kwa munthu wachiwawa.
49Chifukwa chake Yehova ndidzakuyamikani mwa amitundu,
ndipo dzina lanu ndidzaliimbira.
50 2Sam. 7.13, 29; Mas. 144.10 Alanditsa mfumu yake ndi chipulumutso chachikulu;
nachitira chifundo wodzozedwa wake,
Davide, ndi mbumba yake, kunthawi zonse.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.