MASALIMO 32 - Buku Lopatulika Bible 2014

Mwai wa munthu amene Mulungu wamkhululukiraSalimo la Davide. Chilangizo.

1 Mas. 85.2-3; Aro. 4.6-8 Wodala munthuyo wokhululukidwa tchimo lake;

wokwiriridwa choipa chake.

2 Yob. 1.7 Wodala munthuyu Yehova samwerengera mphulupulu zake;

ndimo mumzimu mwake mulibe chinyengo.

3Pamene ndinakhala chete mafupa anga anakalamba

ndi kubuula kwanga tsiku lonse.

4 1Sam. 5.6-7 Chifukwa usana ndi usiku dzanja lanu linandilemera ine;

uwisi wanga unasandulika kuuma kwa malimwe.

5 Luk. 15.18, 21; 1Yoh. 1.9 Ndinavomera choipa changa kwa Inu;

ndipo mphulupulu yanga sindinaibisa.

Ndinati, Ndidzaululira Yehova machimo anga;

ndipo munakhululukira choipa cha kulakwa kwanga.

6 Mas. 69.1; Yes. 55.6 Chifukwa chake oyera mtima onse apemphere kwa Inu,

pa nthawi ya kupeza Inu;

indetu pakusefuka madzi aakulu

sadzamfikira iye.

7 Eks. 15.1-18; Ower. 5.1-31; Mas. 119.114 Inu ndinu mobisalira mwanga;

m'nsautso mudzandisunga;

mudzandizinga ndi nyimbo za chipulumutso.

8 Mas. 25.4 Ine ndidzakulangiza ndi kuphunzitsa iwe za njira ukayendayo;

ndidzakupangira ndi diso langa lakuyang'ana iwe.

9 Miy. 26.3; Yak. 3.3 Musakhale monga kavalo, kapena ngati bulu, wopanda nzeru;

zomangira zao ndizo cham'kamwa ndi chapamutu zakuwakokera,

pakuti ukapanda kutero sadzakuyandikiza.

10 Miy. 13.21; Yer. 17.7; Aro. 2.9 Zisoni zambiri zigwera woipa;

koma chifundo chidzamzinga iye wakukhulupirira Yehova.

11 Mas. 64.10 Sekerani mwa Yehova, ndimo kondwerani inu olungama mtima;

ndipo fuulani mokondwera nonsenu oongoka mtima.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help