MASALIMO 2 - Buku Lopatulika Bible 2014

Ufumu wa wodzozedwa wa Yehova

1

nalingiriranji anthu zopanda pake?

2Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi,

nachita upo akulu pamodzi,

Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wake, ndi kuti,

3 Luk. 19.14 Tidule zomangira zao,

titaye nsinga zao.

4 Miy. 1.8 Wokhala m'mwambayo adzaseka;

Ambuye adzawanyoza.

5Pomwepo adzalankhula nao mu mkwiyo wake,

nadzawaopsa m'ukali wake.

6Koma Ine ndadzoza mfumu yanga

Pa Ziyoni, phiri langa loyera.

7 Mac. 13.33; Aheb. 1.5 Ndidzauza za chitsimikizo:

Yehova ananena ndi Ine,

Iwe ndiwe Mwana wanga; Ine lero ndakubala.

8 Mas. 72.8 Undifunse, ndipo ndidzakupatsa amitundu

akhale cholowa chako,

ndi malekezero a dziko lapansi akhale akoako.

9 Chiv. 2.27 Udzawathyola ndi ndodo yachitsulo;

udzawaphwanya monga mbiya ya woumba.

10Tsono, mafumu inu, chitani mwanzeru;

langikani, oweruza inu a dziko lapansi.

11 Aheb. 12.28 Tumikirani Yehova ndi mantha,

ndipo kondwerani ndi chinthenthe.

12 Mas. 34.8; Yer. 17.7; Yoh. 5.23; Aro. 9.33 Mpsompsoneni Mwanayo, kuti angakwiye,

ndipo mungatayike m'njira

ukayaka pang'ono pokha mkwiyo wake.

Odala onse akumkhulupirira Iye.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help