MASALIMO 28 - Buku Lopatulika Bible 2014

Apempha chipulumutso, ayamika populumutsidwaSalimo la Davide.

1 Mas. 83.1 Kwa Inu, Yehova, ndidzafuulira;

thanthwe langa, musandikhalire ngati wosamva;

pakuti ngati munditontholera ine,

ndidzafanana nao iwo akutsikira kumanda.

2 1Maf. 8.22, 28-29 Mverani mau a kupemba kwanga, pamene ndilirira Inu,

pamene ndikweza manja anga kuloza ponenera panu poyera.

3Musandikoke kundichotsa pamodzi ndi oipa,

ndi ochita zopanda pake;

amene alankhula zamtendere ndi anansi ao,

koma mumtima mwao muli choipa.

4 2Tim. 4.14 Muwapatse monga mwa ntchito zao,

ndi monga mwa choipa chochita iwo;

muwapatse monga mwa machitidwe a manja ao;

muwabwezere zoyenera iwo.

5 Yes. 5.12 Pakuti sasamala ntchito za Yehova,

kapena machitidwe a manja ake,

adzawapasula, osawamanganso.

6Wodalitsika Yehova, Pakuti adamva mau a kupemba kwanga.

7 Mas. 3.3 Yehova ndiye mphamvu yanga, ndi chikopa changa;

mtima wanga wakhulupirira Iye, ndipo anandithandiza,

chifukwa chake mtima wanga ukondwera kwakukulu;

ndipo ndidzamyamika nayo nyimbo yanga.

8Yehova ndiye mphamvu yao,

inde mphamvu ya chipulumutso cha wodzozedwa wake.

9 Mas. 78.71 Pulumutsani anthu anu, ndi kudalitsa cholandira chanu;

muwawetenso, ndi kuwanyamula nthawi zonse.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help