1 Mas. 33.20 Moyo wanga ukhalira chete Mulungu yekha;
chipulumutso changa chifuma kwa Iye.
2 Mas. 18.2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;
msanje wanga, sindidzagwedezeka kwakukulu.
3Mudzamvumvulukira munthu mpaka liti,
kumupha iye, nonsenu,
monga khoma lopendekeka, ndi mpanda woweyeseka?
4 Mas. 28.3 Komatu amkhalira upo kuti amkankhire pansi ulemu wake;
akondwera nao mabodza;
adalitsa ndi m'kamwa mwao,
koma atemberera mumtima.
5Moyo wanga, ukhalire chete Mulungu yekha;
pakuti chiyembekezo changa chifuma kwa Iye.
6Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa,
msanje wanga, sindidzagwedezeka.
7 Yer. 3.23 Pa Mulungu pali chipulumutso changa ndi ulemerero wanga.
Thanthwe la mphamvu yanga ndi pothawirapo panga mpa Mulungu.
8 1Sam. 1.15; Mas. 42.4 Khulupirirani pa Iye nyengo zonse, anthu inu,
tsanulirani mitima yanu pamaso pake.
Mulungu ndiye pothawirapo ife.
9 Yes. 40.15, 17 Indetu, anthu achabe ndi mpweya, ndipo anthu akulu ndi bodza,
pakuwayesa apepuka;
onse pamodzi apepuka koposa mpweya.
10 Luk. 12.15 Musakhulupirire kusautsa, ndipo musatama chifwamba;
chikachuluka chuma musakhazikepo mitima yanu.
11 Chiv. 19.1 Mulungu ananena kamodzi, ndinachimva kawiri,
kuti mphamvu ndi yake ya Mulungu.
12 Mas. 103.8; Miy. 24.12; Yer. 32.19; Mat. 16.27; Aef. 6.8; Akol. 3.25 Chifundonso ndi chanu, Ambuye,
Chifukwa Inu mubwezera munthu aliyense
monga mwa ntchito yake.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.