1 Mas. 35.1; 1Sam. 24.15 Mundiweruzire, Mulungu, ndipo mundinenere mlandu kwa anthu opanda chifundo.
Mundilanditse kwa munthu wonyenga ndi wosalungama.
2 Mas. 42.9 Pakuti Inu ndinu Mulungu wa mphamvu yanga; mwanditayiranji?
Ndimayenderanji woliralira chifukwa cha kundipsinja mdani?
3 Mas. 27.1 Tumizirani kuunika kwanu ndi choonadi chanu zinditsogolere;
zindifikitse kuphiri lanu loyera,
kumene mukhala Inuko.
4Kuti ndipite kufikira guwa la nsembe la Mulungu,
kufikira Mulungu wa chimwemwe changa chenicheni,
ndi kuti ndikuyamikeni ndi zeze, Mulungu, Mulungu wanga.
5 Mas. 42.5, 11 Udziweramiranji moyo wanga iwe?
Ndi kuzingwa m'kati mwanga?
Yembekeza Mulungu: pakuti ndidzamyamikanso,
ndiye chipulumutso cha nkhope yanga, ndi Mulungu wanga.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.