MASALIMO 150 - Buku Lopatulika Bible 2014

Zolengedwa zonse zilemekeze Mulungu

1 Aleluya.

Lemekezani Mulungu m'malo ake oyera;

mlemekezeni m'thambo la mphamvu yake.

2 Mas. 145.5-6 Mlemekezeni chifukwa cha ntchito zake zolimba;

mlemekezeni monga mwa ukulu wake waunjinji.

3Mlemekezeni ndi kulira kwa lipenga;

mlemekezeni ndi chisakasa ndi zeze.

4 Eks. 15.20; Yes. 38.20 Mlemekezeni ndi lingaka ndi kuthira mang'ombe:

Mlemekezeni ndi zoimbira za zingwe ndi chitoliro.

5 1Mbi. 15—16; 19; 28 Mlemekezeni ndi nsanje zomveka:

Mlemekezeni ndi nsanje zoliritsa.

6 Mas. 145.21 Zonse zakupuma zilemekeze Yehova.

Aleluya.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help