1
Anthu amene sindinawadziwa adzanditumikira ine.
45Alendo adzandigonjera ine,
pakumva za ine, adzandimvera pomwepo.
46Alendo adzafota,
nadzabwera ndi kunthunthumira otuluka mokwiririka mwao.
47 Eks. 15.2 Yehova ali ndi moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;
ndipo akulitsidwe Mulungu wa thanthwe la chipulumutso changa;
48inde Mulungu wakundibwezera chilango ine,
ndi kundigonjetsera anthu a mitundu.
49Amene anditulutsa kwa adani anga;
inde mundikweza ine pamwamba pa iwo akundiukira;
mundipulumutsa kwa munthu wachiwawa.
50 Aro. 15.9 Chifukwa chake ndidzakuongani Yehova, pakati pa amitundu,
ndipo ndidzaimba zolemekeza dzina lanu.
51 Mas. 89.20, 29 Iye apatsa mfumu yake chipulumutso chachikulu;
naonetsera chifundo wodzozedwa wake,
kwa Davide ndi mbeu yake ku nthawi zonse.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.