YOSWA 16 - Buku Lopatulika Bible 2014

Malire a Efuremu

1Ndipo gawo la ana a Yosefe linatuluka kuchokera ku Yordani ku Yeriko, ku madzi a Yeriko kum'mawa, kuchipululu, nakwera kuchokera ku Yeriko kunka kumapiri ku Betele;

2natuluka ku Betele kunka ku Luzi, napitirira kunka ku malire a Aariki, ku Ataroti;

3natsikira kumadzulo kunka ku malire a Ayafileti, ku malire a Betehoroni wa kunsi, ndi ku Gezere; ndi matulukiro ake anali kunyanja.

4Motero ana a Yosefe, Manase ndi Efuremu analandira cholowa chao,

5Ndipo malire a ana a Efuremu, monga mwa mabanja ao, ndiwo: malire a cholowa chao kum'mawa ndiwo Ataroti-Adara, mpaka Betehoroni wa kumtunda;

6natuluka malire kumadzulo ku Mikametati kumpoto; nazungulira malire kum'mawa kunka ku Taanatisilo, naupitirira kum'mawa kwake kwa Yanowa:

7natsika kuchokera ku Yanowa, kunka ku Ataroti, ndi ku Naara, nafika ku Yeriko, natuluka ku Yordani.

8Kuyambira ku Tapuwa malire anamuka kumadzulo ku mtsinje wa Kana; ndi matulukiro ake anali kunyanja. Ichi ndi cholowa cha fuko la ana a Efuremu monga mwa mabanja ao;

9pamodzi ndi midzi adaipatulira ana a Efuremu pakati pa cholowa cha ana a Manase, midzi yonse pamodzi ndi milaga yao.

101Maf. 9.16Ndipo sanaingitse Akanani akukhala m'Gezere; koma Akanani anakhala pakati pa Efuremu, kufikira lero lino, nawaumiriza kugwira ntchito yathangata.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help