MASALIMO 118 - Buku Lopatulika Bible 2014

Wa Salimo alemekeza Mulungu womlanditsa m'manja mwa adani

1 1Mbi. 16.8, 34 Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino;

pakuti chifundo chake nchosatha.

2 Mas. 115.9, 11 Anene tsono Israele,

kuti chifundo chake nchosatha.

3Anene tsono nyumba ya Aroni,

kuti chifundo chake nchosatha.

4Anene tsono iwo akuopa Yehova,

kuti chifundo chake nchosatha.

5 Mas. 56.13 M'mene ndinasautsika ndinaitanira pa Yehova;

anandiyankha nandiika motakasuka Yehova.

6 Yes. 51.12; Aheb. 13.6 Yehova ndi wanga; sindidzaopa;

adzandichitanji munthu?

7 Mas. 54.4 Yehova ndi wanga, mwa iwo akundithandiza;

m'mwemo ndidzaona chofuna ine pa iwo akundida.

8 Yer. 17.5, 7 Kuthawira kwa Yehova nkokoma

koposa kukhulupirira munthu.

9 Mas. 146.3 Kuthawira kwa Yehova nkokoma

koposa kukhulupirira akulu.

10 Amitundu onse adandizinga,

zedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

11Adandizinga, inde, adandizinga:

Indedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

12 Deut. 1.44 Adandizinga ngati njuchi;

anazima ngati moto waminga;

indedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

13Kundikankha anandikankha ndikadagwa;

koma Yehova anandithandiza.

14 Yes. 12.2 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;

ndipo anakhala chipulumutso changa.

15M'mahema a olungama muli liu lakufuula mokondwera

Dzanja lamanja la Yehova ndi la chipulumutso:

16Dzanja lamanja la Yehova likwezeka,

Dzanja lamanja la Yehova lichita mwamphamvu.

17 Hab. 1.12 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo,

ndipo ndidzafotokozera ntchito za Yehova.

18 2Ako. 6.9 Kulanga anandilangadi Yehova:

koma sanandipereke kuimfa ai.

19 Yes. 26.2 Nditsegulireni zipata za chilungamo;

ndidzalowamo, ndidzayamika Yehova.

20Chipata cha Yehova ndi ichi;

olungama adzalowamo.

21 Mas. 116.1 Ndidzakuyamikani, popeza munandiyankha,

ndipo munakhala chipulumutso changa.

22 Mat. 21.42; Mrk. 12.10; Luk. 20.17; Mac. 4.11; Aef. 2.20 Mwala umene omangawo anaukana

wakhala mutu wa pangodya.

23Ichi chidzera kwa Yehova;

nchodabwitsa ichi pamaso pathu.

24Tsiku ili ndilo adaliika Yehova;

tidzasekera ndi kukondwera m'mwemo.

25Tikupemphani, Yehova, tipulumutseni tsopano;

tikupemphani, Yehova, tipindulitseni tsopano.

26 Mat. 21.9; 23.39 Wodala wakudzayo m'dzina la Yehova;

takudalitsani kochokera m'nyumba ya Yehova.

27Yehova ndiye Mulungu, amene anatiunikira;

mangani nsembe ndi zingwe, kunyanga za guwa la nsembe.

28 Yes. 25.1 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani;

ndinu Mulungu wanga, ndidzakukwezani.

29 Mas. 118.1 Yamikani Yehova, pakuti Iye ndiye wabwino,

pakuti chifundo chake nchosatha.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help