YOBU 35 - Buku Lopatulika Bible 2014

Elihu akuti kwa Mulungu kulibe chifukwa cha kuchita tsankho

1Ndipo Elihu anabwereza kunena, nati,

2Kodi muchiyesa choyenera,

umo mukuti, Chilungamo changa chiposa cha Mulungu,

3pakuti munena, Upindulanji nacho?

Posachimwa ndinapindula chiyani

chimene sindikadapindula pochimwa?

4Ndidzakuyankhani,

ndi anzanu pamodzi ndi inu.

5Yang'anani kumwamba, nimuone,

tapenyani mitambo yokwera yakuposa inu.

6 Miy. 8.36; Yer. 7.19 Ngati mwachimwa, mumchitira Iye chiyani?

Zikachuluka zolakwa zanu, mumchitira Iye chiyani?

7 Aro. 11.35 Mukakhala wolungama, mumninkhapo chiyani?

Kapena alandira chiyani pa dzanja lanu?

8Choipa chanu chikhoza kuipira munthu wonga inu,

ndi chilungamo chanu chikhoza kukomera wobadwa ndi munthu.

9 Eks. 2.23 Chifukwa cha kuchuluka masautso anthu anafuula,

afuula chifukwa cha dzanja la amphamvu.

10 Mas. 42.8 Koma palibe anganene, Ali kuti Mulungu Mlengi wanga,

wakupatsa nyimbo usiku;

11wakutilangiza ife koposa nyama za padziko,

wakutipatsa nzeru zoposa mbalame za m'mlengalenga?

12Apo afuula, koma Iye sawayankha;

chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oipa.

13 Yer. 11.11 Zedi Mulungu samvera zachabe,

ndi Wamphamvuyonse sazisamalira.

14 Mas. 37.5-6 Inde mungakhale munena, Sindimpenya,

mlanduwo uli pamaso pake, ndipo mumlindira.

15Ndipo tsopano popeza analibe kumzonda m'kukwiya kwake,

ndi kusamalitsa cholakwa,

16chifukwa chake Yobu anatsegula pakamwa pake mwachabe,

nachulukitsa mau opanda nzeru.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help