MASALIMO 47 - Buku Lopatulika Bible 2014

Mau a kulemekeza Mulungu mwini dziko lonse lapansiKwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la ana a Kora.

1 Yes. 55.12 Ombani m'manja, mitundu yonse ya anthu;

fuulirani kwa Mulungu ndi liu la kuimbitsa.

2 Mala. 1.14 Pakuti Yehova Wam'mwambamwamba ndiye woopsa;

ndiye mfumu yaikulu pa dziko lonse lapansi.

3Atigonjetsera anthu,

naika amitundu pansi pa mapazi athu.

4 1Pet. 1.4 Atisankhira cholowa chathu,

chokometsetsa cha Yakobo amene anamkonda.

5Mulungu wakwera ndi mfuu,

Yehova ndi liu la lipenga.

6Imbirani Mulungu, imbirani;

imbirani mfumu yathu, imbirani.

7 Zek. 14.9 Pakuti Mulungu ndiye mfumu ya dziko lonse lapansi;

imbirani ndi chilangizo.

8 Mas. 22.28; Chiv. 19.6 Mulungu ndiye mfumu ya amitundu,

Mulungu akhala pa mpando wachifumu wake woyera.

9 Aro. 4.11-12 Akulu a anthu asonkhana

akhale anthu a Mulungu wa Abrahamu,

pakuti zikopa za dziko lapansi nza Mulungu;

akwezeka kwakukulu Iyeyo.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help