MASALIMO 130 - Buku Lopatulika Bible 2014

Pemphero lakuti akhululukidweNyimbo yokwerera.

1 Mali. 3.55; Yon. 2.2 M'mozamamo ndinakufuulirani, Yehova.

2Ambuye, imvani liu langa;

makutu anu akhale chimverere

mau a kupemba kwanga.

3 Aro. 3.20, 23-24 Mukasunga mphulupulu, Yehova,

adzakhala chilili ndani, Ambuye?

4 Eks. 34.7; 1Maf. 8.39-40 Koma kwa Inu kuli chikhululukiro,

kuti akuopeni.

5 Yes. 8.17 Ndilindira Yehova, moyo wanga ulindira,

ndiyembekeza mau ake.

6 Mas. 63.6 Moyo wanga uyang'anira Ambuye,

koposa alonda matanda kucha;

inde koposa alonda matanda kucha.

7 Mas. 131.3; Yes. 55.7 Israele, uyembekezere Yehova;

chifukwa kwa Yehova kuli chifundo,

kwaonso kuchulukira chiombolo.

8 Mat. 1.21 Ndipo adzaombola Israele

ku mphulupulu zake zonse.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help