MASALIMO 30 - Buku Lopatulika Bible 2014

Mkwiyo wa Mulungu ukhala kanthawi, kuyanja kwao ndi kosathaSalimo la Davide. Nyimbo yakuperekera nyumba kwa Mulungu.

1Ndidzakukwezani, Yehova; pakuti mwandinyamutsa,

ndipo simunandikondwetsera adani anga.

2 Mas. 103.3 Yehova, Mulungu wanga,

ndinafuulira kwa Inu, ndipo munandichiritsa.

3Yehova munabweza moyo wanga kumanda,

munandisunga ndi moyo, kuti ndingatsikire kudzenje.

4 1Mbi. 16.4-5 Imbirani Yehova, inu okondedwa ake,

ndipo yamikani pokumbukira chiyero chake.

5 Yes. 54.7-8; 2Ako. 4.17 Pakuti mkwiyo wake ukhala kanthawi kokha;

koma kuyanja kwake moyo wonse.

Kulira kuchezera,

koma mamawa kuli kufuula kokondwera.

6Ndipo ine, ndinanena m'phindu langa,

sindidzagwedezeka nthawi zonse.

7 Mas. 104.29 Inu, Yehova, munakhazikitsa phiri langa ndi kuyanja kwanu;

munabisa nkhope yanu; ndinaopa.

8Ndinafuulira kwa Inu, Yehova;

kwa Yehova ndinapemba,

9 Mas. 88.11; Yes. 38.18 M'mwazi mwanga muli phindu lanji,

potsikira ine kudzenje?

Ngati fumbi lidzayamika Inu?

Ngati lidzalalikira choonadi chanu?

10Mverani, Yehova, ndipo ndichitireni chifundo,

Yehova, mundithandize ndi Inu.

11 Yes. 61.3 Munasanduliza kulira kwanga kukhale kusekera;

munandivula chiguduli changa, ndipo munandiveka chikondwero,

12kuti ulemu wanga uimbire Inu, wosakhala chete.

Yehova Mulungu wanga, ndidzakuyamikani nthawi zonse.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help