MASALIMO 26 - Buku Lopatulika Bible 2014

Davide popempha Mulungu amweruze, atchula zokoma zakeSalimo la Davide.

1 2Maf. 20.3 Mundiweruze, Yehova, pakuti ndayenda m'ungwiro wanga,

ndipo ndakhulupirira Yehova, sindadzaterereka.

2 Mas. 139.23 Mundiyesere, Yehova, ndipo mundisunthe;

yeretsani impso zanga ndi mtima wanga.

3 2Maf. 20.3 Pakuti chifundo chanu chili pamaso panga;

ndipo ndayenda m'choona chanu.

4 Mas. 1.1; Yer. 15.17 Sindinakhala pansi ndi anthu achabe;

kapena kutsagana nao anthu othyasika.

5Ndidana nao msonkhano wa ochimwa,

ndipo sindidzakhala nao pansi ochita zoipa.

6 Deut. 21.6 Ndidzasamba manja anga mosalakwa;

kuti ndizungulire guwa la nsembe lanu, Yehova;

7kuti ndimveketse mau a chiyamiko,

ndi kulalikira ntchito zanu zonse zozizwa.

8 Mas. 27.4 Yehova, ndikonda chikhalidwe cha nyumba yanu,

ndi malo akukhalamo ulemerero wanu.

9Musandichotsere mzimu wanga pamodzi ndi olakwa,

kapena moyo wanga pamodzi ndi anthu okhetsa mwazi;

10 Yes. 33.15-16 amene m'manja mwao muli mphulupulu,

ndi dzanja lao lamanja ladzala ndi zokometsera mlandu.

11Koma ine, ndidzayenda m'ungwiro wanga;

mundiombole, ndipo ndichitireni chifundo.

12 Mas. 40.2 Phazi langa liponda pachidikha,

m'masonkhano ndidzalemekeza Yehova.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help