1
mukapeza bwenzi langa, mudzamuuza chiyani?
Kuti ndadwala ndi chikondi.
9Bwenzi lako aposa abwenzi ena bwanji,
mkaziwe woposa kukongola?
Bwenzi lako aposa abwenzi ena bwanji,
kuti utilumbirira motero?
10 Mas. 45.2; Yoh. 1.14 Wokondedwa wanga ali woyera ndi wofiira,
womveka mwa zikwi khumi.
11Mutu wake ukunga golide, woyengetsa,
tsitsi lake lopotana, ndi lakuda ngati khungubwi.
12Ana a maso ake akunga nkhunda
pambali pa mitsinje ya madzi;
otsukidwa ndi mkaka, okhala pa mitsinje yodzala.
13Masaya ake akunga chitipula chobzalamo ndiwo,
ngati mitumbira yoyangapo masamba onunkhira:
Milomo yake ikunga akakombo, pakukhapo madzi a mure.
14Manja ake akunga zing'anda zagolide
zoikamo zonyezimira zoti biriwiri.
Thupi lake likunga chopanga cha minyanga
cholemberapo masafiro.
15Miyendo yake ikunga zoimiritsa za mwala wonyezimira,
zogwirika m'kamwa mwa golide:
Maonekedwe ake akunga Lebanoni,
okometsetsa ngati mikungudza.
16M'kamwa mwake muli mokoma; inde,
ndiye wokondweretsa ndithu.
Ameneyu ndi wokondedwa wanga,
ameneyu ndi bwenzi langa,
ana akazi inu a ku Yerusalemu.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.