NYIMBO YA SOLOMONI 5 - Buku Lopatulika Bible 2014

1

mukapeza bwenzi langa, mudzamuuza chiyani?

Kuti ndadwala ndi chikondi.

9Bwenzi lako aposa abwenzi ena bwanji,

mkaziwe woposa kukongola?

Bwenzi lako aposa abwenzi ena bwanji,

kuti utilumbirira motero?

10 Mas. 45.2; Yoh. 1.14 Wokondedwa wanga ali woyera ndi wofiira,

womveka mwa zikwi khumi.

11Mutu wake ukunga golide, woyengetsa,

tsitsi lake lopotana, ndi lakuda ngati khungubwi.

12Ana a maso ake akunga nkhunda

pambali pa mitsinje ya madzi;

otsukidwa ndi mkaka, okhala pa mitsinje yodzala.

13Masaya ake akunga chitipula chobzalamo ndiwo,

ngati mitumbira yoyangapo masamba onunkhira:

Milomo yake ikunga akakombo, pakukhapo madzi a mure.

14Manja ake akunga zing'anda zagolide

zoikamo zonyezimira zoti biriwiri.

Thupi lake likunga chopanga cha minyanga

cholemberapo masafiro.

15Miyendo yake ikunga zoimiritsa za mwala wonyezimira,

zogwirika m'kamwa mwa golide:

Maonekedwe ake akunga Lebanoni,

okometsetsa ngati mikungudza.

16M'kamwa mwake muli mokoma; inde,

ndiye wokondweretsa ndithu.

Ameneyu ndi wokondedwa wanga,

ameneyu ndi bwenzi langa,

ana akazi inu a ku Yerusalemu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help