NYIMBO YA SOLOMONI 2 - Buku Lopatulika Bible 2014

1Ndine duwa lofiira la ku Saroni,

ngakhale kakombo wa kuzigwa.

2Ngati kakombo pakati pa minga

momwemo wokondedwa wanga pakati pa ana akazi.

3Ngati maula pakati pa mitengo ya m'nkhalango,

momwemo wokondedwa wanga pakati pa ana amuna.

Ndinakondwa pakukhala pa mthunzi wake,

zipatso zake zinatsekemera m'kamwa mwanga.

4

pali mphoyo, ndi mbawala za kuthengo,

kuti musautse, ngakhale kugalamutsa chikondi,

mpaka chikafuna mwini.

8Mau a wokondedwa wanga mnyamatayo! Taona, adza,

alikulumpha pamapiri, alikujidimuka pazitunda.

9Wokondedwa wanga akunga mphoyo,

pena mwana wa mbawala:

Taona, aima patseri pakhoma lathu.

Apenyera pazenera,

nasuzumira pamade.

10Wokondedwa wanga analankhula, nati kwa ine,

tauka, bwenzi langa, wokongola wanga, tiye.

11Pakuti, taona, chisanu chatha,

mvula yapita yaleka;

12maluwa aoneka pansi;

nthawi yoimba mbalame yafika,

mau a njiwa namveka m'dziko lathu.

13Mkuyu utchetsa nkhuyu zake zosakhwima,

mipesa niphuka,

inunkhira bwino.

Tauka, bwenzi langa, wokongola wangawe, tiyetu.

14Nkhunda yangawe, yokhala m'ming'alu ya thanthwe,

mobisika motsetsereka,

ndipenye nkhope yako, ndimve mau ako;

pakuti mau ako ngokoma, nkhope yako ndi kukongola.

15 1Ako. 5.6 Mutigwirire ankhandwe, ngakhale ang'ono,

amene akuononga minda yamipesa;

pakuti m'minda yathu yamipesa muphuka biriwiri.

16 Nyi. 6.3 Wokondedwa wanga ndi wa ine, ine ndine wake:

aweta zake pakati akakombo.

17Mpaka dzuwa litapepa, mithunzi ndi kutanimpha,

bwera, bwenzi langawe, nukhale ngati mphoyo

pena mwana wa mbawala

pa mapiri a mipata.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help