1Ndine duwa lofiira la ku Saroni,
ngakhale kakombo wa kuzigwa.
2Ngati kakombo pakati pa minga
momwemo wokondedwa wanga pakati pa ana akazi.
3Ngati maula pakati pa mitengo ya m'nkhalango,
momwemo wokondedwa wanga pakati pa ana amuna.
Ndinakondwa pakukhala pa mthunzi wake,
zipatso zake zinatsekemera m'kamwa mwanga.
4
pali mphoyo, ndi mbawala za kuthengo,
kuti musautse, ngakhale kugalamutsa chikondi,
mpaka chikafuna mwini.
8Mau a wokondedwa wanga mnyamatayo! Taona, adza,
alikulumpha pamapiri, alikujidimuka pazitunda.
9Wokondedwa wanga akunga mphoyo,
pena mwana wa mbawala:
Taona, aima patseri pakhoma lathu.
Apenyera pazenera,
nasuzumira pamade.
10Wokondedwa wanga analankhula, nati kwa ine,
tauka, bwenzi langa, wokongola wanga, tiye.
11Pakuti, taona, chisanu chatha,
mvula yapita yaleka;
12maluwa aoneka pansi;
nthawi yoimba mbalame yafika,
mau a njiwa namveka m'dziko lathu.
13Mkuyu utchetsa nkhuyu zake zosakhwima,
mipesa niphuka,
inunkhira bwino.
Tauka, bwenzi langa, wokongola wangawe, tiyetu.
14Nkhunda yangawe, yokhala m'ming'alu ya thanthwe,
mobisika motsetsereka,
ndipenye nkhope yako, ndimve mau ako;
pakuti mau ako ngokoma, nkhope yako ndi kukongola.
15 1Ako. 5.6 Mutigwirire ankhandwe, ngakhale ang'ono,
amene akuononga minda yamipesa;
pakuti m'minda yathu yamipesa muphuka biriwiri.
16 Nyi. 6.3 Wokondedwa wanga ndi wa ine, ine ndine wake:
aweta zake pakati akakombo.
17Mpaka dzuwa litapepa, mithunzi ndi kutanimpha,
bwera, bwenzi langawe, nukhale ngati mphoyo
pena mwana wa mbawala
pa mapiri a mipata.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.