MASALIMO 4 - Buku Lopatulika Bible 2014

Pemphero posautsidwaKwa Mkulu wa Nyimbo; pa Neginoto. Salimo la Davide.

1Pakufuula ine mundiyankhe, Mulungu wa chilungamo changa;

pondichepera mwandikulitsira malo.

Ndichitireni chifundo, imvani pemphero langa.

2Amuna inu, ulemu wanga udzakhala wamanyazi kufikira liti?

Mudzakonda zachabe, ndi kufunafuna bodza kufikira liti?

3 2Tim. 2.19 Koma dziwani kuti Yehova anadzipatulira yekha womkondayo,

adzamva Yehova m'mene ndimfuulira Iye.

4 2Ako. 13.5; Aef. 4.26 Chitani chinthenthe, ndipo musachimwe.

Nenani mumtima mwanu pakama panu, ndipo mukhale chete.

5 Mas. 51.19 Iphani nsembe za chilungamo,

ndipo mumkhulupirire Yehova.

6 Num. 6.26 Ambiri amati, Adzationetsa chabwino ndani?

Weramutsirani ife kuunika kwa nkhope yanu, Yehova.

7 Yes. 9.3 Mwapatsa chimwemwe mumtima mwanga,

chakuposa chao m'nyengo yakuchuluka dzinthu zao ndi vinyo wao.

8 Mas. 3.5 Ndi mtendere ndidzagona pansi, pomwepo ndidzagona tulo;

chifukwa Inu, Yehova, mundikhalitsa ine, ndikhale bwino.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help