MASALIMO 142 - Buku Lopatulika Bible 2014

Pemphero pakuopsedwa kwakukuluChilangizo cha Davide, muja anakhala m'phanga; Pemphero.

1Ndifuula nalo liu langa kwa Yehova;

ndi mau anga ndipemba kwa Yehova.

2 Yes. 26.16 Nditsanulira kudandaula kwanga pamaso pake;

ndionetsa msauko wanga pamaso pake.

3 Mas. 141.9 Pamene mzimu wanga unakomoka m'kati mwanga, munadziwa njira yanga.

M'njira ndiyendamo ananditchera msampha.

4 Mas. 31.11 Penyani kudzanja lamanja ndipo muone; palibe wondidziwa;

pothawirapo pandisowa; palibe mmodzi wosamalira moyo wanga.

5 Mas. 46.1 Ndinafuulira kwa inu, Yehova;

ndinati, Inu ndinu pothawirapo panga,

gawo langa m'dziko la amoyo.

6 Mas. 116.6 Tamverani kufuula kwanga; popeza ndisauka kwambiri;

ndilanditseni kwa iwo akundilondola; popeza andilaka.

7Tulutsani moyo wanga m'ndende, kuti ndiyamike dzina lanu;

olungama adzandizinga;

pakuti mudzandichitira zokoma.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help