NYIMBO YA SOLOMONI 4 - Buku Lopatulika Bible 2014

Mkwati alemekeza mkwatibwi

1Taona, wakongola, bwenzi langa,

namwaliwe, taona, wakongola;

maso ako akunga a nkhunda patseri pa chophimba chako.

Tsitsi lako likunga gulu la mbuzi,

zooneka pa phiri la Giliyadi.

2Mano ako akunga gulu la nkhosa zosengasenga,

zokwera kuchokera kosamba;

yonse ili ndi ana awiri,

palibe imodzi yopoloza.

3Milomo yako ikunga mbota yofiira,

m'kamwa mwako ndi kukoma:

Palitsipa pako pakunga phande la khangaza

paseli pa chophimba chako.

4

ndi kuchitunda cha lubani.

7

14Narido ndi chikasu,

nzimbe ndi sinamoni, ndi mitengo yonse ya lubani;

mure ndi khonje, ndi zonunkhiritsa zonse zomveka.

15 Yes. 49.10; Yoh. 4.10 Ndiwe kasupe wa m'minda,

chitsime cha madzi amoyo,

ndi mitsinje yoyenda yochokera ku Lebanoni.

Ayankha mkwatibwi

16Galamuka, mphepo ya kumpoto iwe,

nudze, mphepo iwe ya kumwera;

nuombe pamunda panga, kuti zonunkhiritsa zake zitulukemo.

Bwenzi langa mnyamatayo, alowe m'munda mwake,

nadye zipatso zake zofunika.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help