MASALIMO 5 - Buku Lopatulika Bible 2014

Matsoka a oipa, madalitso a olungamaKwa Mkulu wa Nyimbo; aimbire zitoliro. Salimo la Davide.

1Mverani mau anga, Yehova, Zindikirani kulingirira kwanga.

2Tamvetsani mau a kufuula kwanga,

Mfumu yanga, ndi Mulungu wanga;

pakuti kwa Inu ndimapemphera.

3 Mas. 88.13 M'mawa, Yehova, mudzamva mau anga;

m'mawa, ndidzakukonzerani pemphero langa, ndipo ndidzadikira.

4Pakuti Inu sindinu Mulungu wakukondwera nacho choipa

mphulupulu siikhala ndi Inu.

5 Hab. 1.13 Opusa sadzakhazikika pamaso panu,

mudana nao onse akuchita zopanda pake.

6 Mas. 55.23 Mudzaononga iwo akunena bodza;

munthu wokhetsa mwazi ndi wachinyengo,

Yehova anyansidwa naye.

7 1Maf. 8.29-30 Koma ine, mwa kuchuluka kwa chifundo chanu

ndidzalowa m'nyumba yanu;

ndidzagwada kuyang'ana Kachisi wanu woyera ndi kuopa Inu.

8 Mas. 25.5 Yehova, munditsogolere m'chilungamo chanu,

chifukwa cha akundizondawo;

mulungamitse njira yanu pamaso panga.

9 Mas. 62.4; Aro. 3.13 Pakuti m'kamwa mwao mulibe mau okhazikika;

m'kati mwao m'mosakaza;

m'mero mwao ndi manda apululu;

lilime lao asyasyalika nalo.

10 2Sam. 15.31 Muwayese otsutsika Mulungu;

agwe nao uphungu wao.

M'kuchuluka kwa zolakwa zao muwapirikitse;

pakuti anapikisana ndi Inu.

11 Yes. 65.13 Koma akondwere onse amene athawira kwa Inu,

afuule mokondwera kosaleka, popeza muwafungatira;

nasekere mwa Inu iwo akukonda dzina lanu.

12Pakuti Inu, Yehova, mudzadalitsa wolungamayo;

mudzamtchinjiriza nacho chivomerezo ngati chikopa.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help