Yesaya 15 - The Word of God in Contemporary Chichewa

Za Kulangidwa kwa Mowabu

1Uthenga wonena za Mowabu:

Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa,

wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.

Mzinda wa Kiri wawonongedwa,

wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.

2Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo,

akupita ku malo awo achipembedzo kukalira;

anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba.

Mutu uliwonse wametedwa mpala,

ndipo ndevu zonse zametedwa.

3Mʼmisewu akuvala ziguduli;

pa madenga ndi mʼmabwalo

aliyense akulira mofuwula,

misozi ili pupupu.

4Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula,

mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi.

Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula,

ndipo ataya mtima.

5Inenso ndikulirira Mowabu;

chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari

ndi Egilati-Selisiya

akupita akulira ku chikweza cha Luhiti,

Akulira mosweka mtima

pa njira yopita ku Horonaimu;

akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.

6Madzi a ku Nimurimu aphwa

ndipo udzu wauma;

zomera zawonongeka

ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.

7Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga,

achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.

8Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu;

kulira kwawo kosweka mtima kukumveka

mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.

9Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi,

komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni,

mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu

ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help