Masalimo 129 - The Word of God in Contemporary Chichewa

Salimo 129Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,”

anene tsono Israeli;

2“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,

koma sanandipambane.

3Anthu otipula analima pa msana panga

ndipo anapangapo mizere yayitali:

4Koma Yehova ndi wolungama;

Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”

5Onse amene amadana ndi Ziyoni

abwezedwe pambuyo mwamanyazi.

6Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba,

umene umafota usanakule;

7sungadzaze manja a owumweta

kapena manja a omanga mitolo.

8Odutsa pafupi asanene kuti,

“Dalitso la Yehova lili pa inu;

tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help