Yoswa 12 - The Word of God in Contemporary Chichewa

Mayina a Mafumu Ogonjetsedwa

1Aisraeli anagonjetsa dziko lonse la kummawa kwa Yorodani, kuyambira ku chigwa cha Arinoni mpaka ku phiri la Herimoni pamodzi ndi dera lonse la kummawa kwa Araba. Iwo anatenga dzikoli kukhala lawo, ndipo mafumu a dzikoli anali awa:

2Sihoni mfumu ya Aamori,

amene ankakhala mu Hesiboni. Iye analamulira kuyambira ku Aroeri mzinda umene uli mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni, mpaka ku mtsinje wa Yaboki, umene uli mʼmalire mwa Aamori, kuphatikizanso theka la dziko la Giliyadi.

3Iye ankalamuliranso dera la chigwa cha Yorodani kuyambira ku Nyanja ya Kinereti, kummawa ndi kumatsika mpaka ku Beti-Yesimoti, mzinda umene unali kummawa kwa Nyanja ya Mchere ndi kutsikabe kummwera mpaka pa tsinde pa phiri la Pisiga.

4Ogi mfumu ya mzinda wa Basani,

amene anali mmodzi mwa otsala mwa Arefaimu. Iye ankakhala ku Asiteroti ndi Ederi.

5Dera la ufumu wake linafika ku phiri la Herimoni, ku Saleka ndi dziko lonse la Basani mpaka ku malire ndi anthu a ku Gesuri Makati. Ufumu wake unaphatikizanso theka la Giliyadi mpaka ku malire a mfumu Sihoni ya ku Hesiboni.

6Mose mtumiki wa Yehova ndi Aisraeli anawagonjetsa ndipo anapereka dziko lawo kwa anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti chikhale cholowa chawo.

7Yoswa ndi Aisraeli onse anagonjetsa mafumu onse okhala kumadzulo kwa mtsinje wa Yorodani kuyambira ku Baala-Gadi, ku chigwa cha Lebanoni mpaka ku phiri la Halaki, kumapita cha ku Seiri. Yoswa anagawira dzikolo mafuko a Israeli kuti likhale cholowa chawo.

8Dziko limeneli linali dera la ku mapiri, chigwa cha kumadzulo, chigwa cha Yorodani, ku matsitso a kummawa, ndi dziko la chipululu la kummwera. Amene ankakhala mʼdzikoli anali Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi. Mafumu ake anali awa:

9mfumu ya Yeriko

imodzi

mfumu ya Ai (kufupi ndi Beteli

imodzi

10mfumu ya Yerusalemu

imodzi

mfumu ya Hebroni

imodzi

11mfumu ya Yarimuti

imodzi

mfumu ya Lakisi

imodzi

12mfumu ya Egiloni

imodzi

mfumu ya Gezeri

imodzi

13mfumu ya Debri

imodzi

mfumu ya Gederi

imodzi

14mfumu ya Horima

imodzi

mfumu ya Aradi

imodzi

15mfumu ya Libina

imodzi

mfumu ya Adulamu

imodzi

16mfumu ya Makeda

imodzi

mfumu ya Beteli

imodzi

17mfumu ya Tapuwa

imodzi

mfumu ya Heferi

imodzi

18mfumu ya Afeki

imodzi

mfumu ya Lasaroni

imodzi

19mfumu ya Madoni

imodzi

mfumu ya Hazori

imodzi

20mfumu ya Simuroni Meroni

imodzi

mfumu ya Akisafu

imodzi

21mfumu ya Taanaki

imodzi

mfumu ya Megido

imodzi

22mfumu ya Kadesi

imodzi

mfumu ya Yokineamu ku Karimeli

imodzi

23mfumu ya Dori ku Nafoti Dori

imodzi

mfumu ya Goyini ku Giligala

imodzi

24mfumu ya Tiriza

imodzi

mafumu onse pamodzi analipo 31.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help