Nehemiya 7 - The Word of God in Contemporary Chichewa

1Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.

2Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.

3Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”

Mndandanda wa Anthu Oyamba Kubwera Kuchokera ku Ukapolo

4Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.

5Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:

6Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.

7Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana.

Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:

8Zidzukulu za Parosi

2,172

9Zidzukulu za Sefatiya

372

10Zidzukulu za Ara

652

11Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu)

2,818

12Zidzukulu za Elamu

1,254

13Zidzukulu za Zatu

845

14Zidzukulu za Zakai

760

15Zidzukulu za Binuyi

648

16Zidzukulu za Bebai

628

17Zidzukulu za Azigadi

2,322

18Zidzukulu za Adonikamu

667

19Zidzukulu za Abigivai

2,067

20Zidzukulu za Adini

655

21Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya)

98

22Zidzukulu za Hasumu

328

23Zidzukulu za Bezayi

324

24Zidzukulu za Harifu

112

25Zidzukulu za Gibiyoni

95.

26Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa

188

27Anthu a ku Anatoti

128

28Anthu a ku Beti-Azimaveti

42

29Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti

743

30Anthu a ku Rama ndi Geba

621

31Anthu a ku Mikimasi

122

32Anthu a ku Beteli ndi Ai

123

33Anthu a ku Nebo winayo

52

34Ana a Elamu wina

1,254

35Zidzukulu za Harimu

320

36Zidzukulu za Yeriko

345

37Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono

721

38Zidzukulu za Senaya

3,930.

39Ansembe anali awa:

A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa)

973

40Zidzukulu za Imeri

1,052

41Zidzukulu za Pasi-Huri

1,247

42Zidzukulu za Harimu

1,017.

43Alevi anali awa:

A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya

74.

44Anthu oyimba:

   Zidzukulu za Asafu

148.

45Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa:

Zidzukulu za

   Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai

138.

46Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa:

Zidzukulu za

   Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,

47Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni

48Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,

49Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,

50Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,

51Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,

52Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,

53Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,

54Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,

55Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema

56Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.

57Zidzukulu za antchito a Solomoni:

Zidzukulu za

   Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida

58zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,

59zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu

   zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.

60Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo

392.

61Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.

62Zidzukulu za

   Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda

642.

63Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa:

zidzukulu za

Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).

64Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.

65Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.

66Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.

67Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.

68Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.

69Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.

70Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.

71Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.

72Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.

73Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo.

Ezara Awerenga Malamulo

Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help