Masalimo 101 - The Word of God in Contemporary Chichewa

Salimo 101Salimo la Davide.

1Ndidzayimba za chikondi ndi chiweruzo chanu cholungama;

kwa Inu Yehova ndidzayimba matamando.

2Ndidzatsata njira yolungama;

nanga mudzabwera liti kwa ine?

Ndidzayenda mʼnyumba mwanga

ndi mtima wosalakwa.

3Sindidzayika chinthu chilichonse choyipa

pamaso panga.

Ine ndimadana ndi zochita za anthu opanda chikhulupiriro;

iwo sadzadziphatika kwa ine.

4Anthu a mtima wokhota adzakhala kutali ndi ine;

ine sindidzalola choyipa chilichonse kulowa mwa ine.

5Aliyense wosinjirira mnansi wake mseri

ameneyo ndidzamuletsa;

aliyense amene ali ndi maso amwano ndi mtima wodzikuza,

ameneyo sindidzamulekerera.

6Maso anga adzakhala pa okhulupirika mʼdziko,

kuti akhale pamodzi ndi ine;

iye amene mayendedwe ake ndi wosalakwa

adzanditumikira.

7Aliyense wochita chinyengo

sadzakhala mʼnyumba mwanga.

Aliyense woyankhula mwachinyengo

sadzayima pamaso panga.

8Mmawa uliwonse ndidzatontholetsa anthu

onse oyipa mʼdziko;

ndidzachotsa aliyense wochita zoyipa

mu mzinda wa Yehova.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help