Masalimo 82 - The Word of God in Contemporary Chichewa

Salimo 82Salimo la Asafu.

1Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;

Iye akuweruza pakati pa “milungu.”

2“Mudzateteza osalungama mpaka liti,

ndi kukondera anthu oyipa?

3Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;

mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.

4Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;

apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.

5“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.

Amayendayenda mu mdima;

maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

6“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,

nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’

7Koma mudzafa ngati anthu wamba;

mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”

8Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,

pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help