Masalimo 100 - The Word of God in Contemporary Chichewa

Salimo 100Salimo. Nyimbo yothokoza.

1Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.

2Mulambireni Yehova mosangalala;

bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.

3Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu.

Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake;

ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.

4Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko

ndi ku mabwalo ake ndi matamando;

muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.

5Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya;

kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help