1Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerako ku ukapolo, amene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anawagwira ukapolo ndi kupita nawo ku Babuloni (iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wake.
2Iwo anabwerera pamodzi ndi Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Seruya, Reelaya, Mordekai, Bilisani, Misipara, Bigivai, Rehumu ndi Baana).
Chiwerengero cha anthu aamuna a Israeli chinali chotere:
3Zidzukulu za Parosi
2,172
4zidzukulu za Sefatiya
372
5zidzukulu za Ara
775
6zidzukulu za Pahati-Mowabu (zochokera kwa Yesuwa ndi Yowabu)
2,812
7zidzukulu za Elamu
1,254
8zidzukulu za Zatu
945
9zidzukulu za Zakai
760
10zidzukulu za Bani
642
11zidzukulu za Bebai
623
12zidzukulu za Azigadi
1,222
13zidzukulu za Adonikamu
666
14zidzukulu za Bigivai
2,056
15zidzukulu za Adini
454
16zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya)
98
17zidzukulu za Bezayi
323
18zidzukulu za Yora
112
19zidzukulu za Hasumu
223
20zidzukulu za Gibari
95.
21Anthu a ku Betelehemu
123
22Anthu aamuna a ku Netofa
56
23Anthu aamuna a ku Anatoti
128
24Anthu aamuna a ku Azimaveti
42
25Anthu aamuna a ku Kiriati Yearimu, Kefira ndi Beeroti
743
26Anthu aamuna a ku Rama ndi Geba
621
27Anthu aamuna a ku Mikimasi
122
28Anthu aamuna a ku Beteli ndi Ai
223
29Anthu aamuna a ku Nebo
52
30Anthu aamuna a ku Magaibisi
156
31Anthu aamuna a ku Elamu wina
1,254
32Anthu aamuna a ku Harimu
320
33Anthu aamuna a ku Lodi, Hadidi ndi Ono
725
34Anthu aamuna a ku Yeriko
345
35Anthu aamuna a ku Sena
3,630.
36Ansembe anali awa:
Zidzukulu za Yedaya (kudzera mu banja la Yesuwa)
973
37Zidzukulu za Imeri
1,052
38Zidzukulu za Pasuri
1,247
39Zidzukulu za Harimu
1,017.
40Alevi anali awa:
Zidzukulu za Yesuwa ndi Kadimieli (kudzera mwa ana a Hodaviya)
74.
41Anthu oyimba nyimbo anali awa:
Zidzukulu za Asafu
128.
42Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa:
Zidzukulu za Salumu, zidzukulu za Ateri, zidzukulu za Talimoni, zidzukulu za Akubu, zidzukulu za Hatita ndi zidzukulu za Sobai
139.
43Otumikira ku Nyumba ya Mulungu anali awa:
Zidzukulu za
Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
44zidzukulu za Kerosi, zidzukulu za Siyaha, Padoni,
45zidzukulu za Lebana, zidzukulu za Hagaba, zidzukulu za Akubu,
46zidzukulu za Hagabu, zidzukulu za Salimayi, zidzukulu za Hanani,
47zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari, zidzukulu za Reaya,
48zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nekoda, zidzukulu za Gazamu,
49zidzukulu za Uza, zidzukulu za Peseya, zidzukulu za Besai,
50zidzukulu za Asina, zidzukulu za Meunimu, Nefusimu,
51zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
52zidzukulu za Baziruti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
53zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema,
54zidzukulu za Neziya ndi zidzukulu za Hatifa.
55Zidzukulu za antchito a Solomoni zinali izi:
Zidzukulu za
Sotai, zidzukulu za Hasofereti, zidzukulu za Peruda,
56zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
57zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu,
zidzukulu za Pokereti, Hazebayimu ndi Ami.
58Chiwerengero cha onse otumikira ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za Solomoni chinali
392.
59Anthu ali mʼmunsiwa anabwera kuchokera ku mizinda ya Teli-Mela, Teli-Harisa, Kerubi, Adoni ndi Imeri, ngakhale samatha kutsimikiza kuti mafuko awo analidi Aisraeli enieni kapena ayi:
60Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya, ndi zidzukulu za Nekoda. Onse pamodzi anali
652.
61Ndi ena pakati pa ansembe anali awa:
Zidzukulu za
Hobiya, Hakozi, ndi Barizilai (Zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai. Barizilai ameneyu ndi uja anakwatira mmodzi mwa ana aakazi a Barizilai Mgiliyadi ndipo ankadziwika ndi dzina la bambo wawoyo.)
62Amenewa anafufuza mayina awo mʼbuku lofotokoza mbiri ya mafuko awo, koma mayinawo sanawapezemo, choncho anawachotsa pa unsembe ngati anthu odetsedwa pa zachipembedzo.
63Bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo mpaka atapezeka wansembe wodziwa kuwombeza ndi Urimu ndi Tumimu.
64Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 42,360,
65kuwonjezera pamenepo, panalinso antchito awo aamuna ndi aakazi okwanira 7,337. Analinso ndi amuna ndi akazi oyimba nyimbo okwanira 200.
66Anali ndi akavalo 736, nyulu 245,
67ngamira 435 ndi abulu 6,720.
68Atafika ku Nyumba ya Yehova mu Yerusalemu, ena mwa atsogoleri a mabanja anapereka zopereka zaufulu zothandizira kumanganso Nyumba ya Mulungu pamalo pake pakale.
69Anapereka kwa msungichuma wa ntchitoyo molingana ndi mmene aliyense chuma chake chinalili: golide wa makilogalamu 500, siliva makilogalamu 2,800 ndi zovala za ansembe zokwanira 100.
70Ansembe, Alevi, oyimba nyimbo, alonda ndi antchito a ku Nyumba ya Yehova pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmidzi ya makolo awo.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.