Ezara 2 - The Word of God in Contemporary Chichewa

Mʼndandanda wa Ayuda amene Anabwerera

1Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerako ku ukapolo, amene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anawagwira ukapolo ndi kupita nawo ku Babuloni (iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wake.

2Iwo anabwerera pamodzi ndi Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Seruya, Reelaya, Mordekai, Bilisani, Misipara, Bigivai, Rehumu ndi Baana).

Chiwerengero cha anthu aamuna a Israeli chinali chotere:

3Zidzukulu za Parosi

2,172

4zidzukulu za Sefatiya

372

5zidzukulu za Ara

775

6zidzukulu za Pahati-Mowabu (zochokera kwa Yesuwa ndi Yowabu)

2,812

7zidzukulu za Elamu

1,254

8zidzukulu za Zatu

945

9zidzukulu za Zakai

760

10zidzukulu za Bani

642

11zidzukulu za Bebai

623

12zidzukulu za Azigadi

1,222

13zidzukulu za Adonikamu

666

14zidzukulu za Bigivai

2,056

15zidzukulu za Adini

454

16zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya)

98

17zidzukulu za Bezayi

323

18zidzukulu za Yora

112

19zidzukulu za Hasumu

223

20zidzukulu za Gibari

95.

21Anthu a ku Betelehemu

123

22Anthu aamuna a ku Netofa

56

23Anthu aamuna a ku Anatoti

128

24Anthu aamuna a ku Azimaveti

42

25Anthu aamuna a ku Kiriati Yearimu, Kefira ndi Beeroti

743

26Anthu aamuna a ku Rama ndi Geba

621

27Anthu aamuna a ku Mikimasi

122

28Anthu aamuna a ku Beteli ndi Ai

223

29Anthu aamuna a ku Nebo

52

30Anthu aamuna a ku Magaibisi

156

31Anthu aamuna a ku Elamu wina

1,254

32Anthu aamuna a ku Harimu

320

33Anthu aamuna a ku Lodi, Hadidi ndi Ono

725

34Anthu aamuna a ku Yeriko

345

35Anthu aamuna a ku Sena

3,630.

36Ansembe anali awa:

   Zidzukulu za Yedaya (kudzera mu banja la Yesuwa)

973

37Zidzukulu za Imeri

1,052

38Zidzukulu za Pasuri

1,247

39Zidzukulu za Harimu

1,017.

40Alevi anali awa:

   Zidzukulu za Yesuwa ndi Kadimieli (kudzera mwa ana a Hodaviya)

74.

41Anthu oyimba nyimbo anali awa:

   Zidzukulu za Asafu

128.

42Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa:

   Zidzukulu za Salumu, zidzukulu za Ateri, zidzukulu za Talimoni, zidzukulu za Akubu, zidzukulu za Hatita ndi zidzukulu za Sobai

139.

43Otumikira ku Nyumba ya Mulungu anali awa:

Zidzukulu za

   Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,

44zidzukulu za Kerosi, zidzukulu za Siyaha, Padoni,

45zidzukulu za Lebana, zidzukulu za Hagaba, zidzukulu za Akubu,

46zidzukulu za Hagabu, zidzukulu za Salimayi, zidzukulu za Hanani,

47zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari, zidzukulu za Reaya,

48zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nekoda, zidzukulu za Gazamu,

49zidzukulu za Uza, zidzukulu za Peseya, zidzukulu za Besai,

50zidzukulu za Asina, zidzukulu za Meunimu, Nefusimu,

51zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,

52zidzukulu za Baziruti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,

53zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema,

54zidzukulu za Neziya ndi zidzukulu za Hatifa.

55Zidzukulu za antchito a Solomoni zinali izi:

Zidzukulu za

   Sotai, zidzukulu za Hasofereti, zidzukulu za Peruda,

56zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,

57zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu,

   zidzukulu za Pokereti, Hazebayimu ndi Ami.

58Chiwerengero cha onse otumikira ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za Solomoni chinali

392.

59Anthu ali mʼmunsiwa anabwera kuchokera ku mizinda ya Teli-Mela, Teli-Harisa, Kerubi, Adoni ndi Imeri, ngakhale samatha kutsimikiza kuti mafuko awo analidi Aisraeli enieni kapena ayi:

60Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya, ndi zidzukulu za Nekoda. Onse pamodzi anali

652.

61Ndi ena pakati pa ansembe anali awa:

Zidzukulu za

   Hobiya, Hakozi, ndi Barizilai (Zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai. Barizilai ameneyu ndi uja anakwatira mmodzi mwa ana aakazi a Barizilai Mgiliyadi ndipo ankadziwika ndi dzina la bambo wawoyo.)

62Amenewa anafufuza mayina awo mʼbuku lofotokoza mbiri ya mafuko awo, koma mayinawo sanawapezemo, choncho anawachotsa pa unsembe ngati anthu odetsedwa pa zachipembedzo.

63Bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo mpaka atapezeka wansembe wodziwa kuwombeza ndi Urimu ndi Tumimu.

64Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 42,360,

65kuwonjezera pamenepo, panalinso antchito awo aamuna ndi aakazi okwanira 7,337. Analinso ndi amuna ndi akazi oyimba nyimbo okwanira 200.

66Anali ndi akavalo 736, nyulu 245,

67ngamira 435 ndi abulu 6,720.

68Atafika ku Nyumba ya Yehova mu Yerusalemu, ena mwa atsogoleri a mabanja anapereka zopereka zaufulu zothandizira kumanganso Nyumba ya Mulungu pamalo pake pakale.

69Anapereka kwa msungichuma wa ntchitoyo molingana ndi mmene aliyense chuma chake chinalili: golide wa makilogalamu 500, siliva makilogalamu 2,800 ndi zovala za ansembe zokwanira 100.

70Ansembe, Alevi, oyimba nyimbo, alonda ndi antchito a ku Nyumba ya Yehova pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmidzi ya makolo awo.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help