Masalimo 67 - The Word of God in Contemporary Chichewa

Salimo 67Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo.

1Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa,

achititse kuti nkhope yake itiwalire.

2Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi,

chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.

3Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;

mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.

4Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe,

pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo

ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.

5Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;

mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.

6Nthaka yabereka zokolola zake;

tidalitseni Mulungu wathu.

7Mulungu atidalitse

kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help