Masalimo 2 - The Word of God in Contemporary Chichewa

Salimo 2

1Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu?

Akonzekeranji zopanda pake anthu?

2Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo;

ndipo olamulira asonkhana pamodzi

kulimbana ndi Ambuye

ndi wodzozedwa wakeyo.

3Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo

ndipo titaye zingwe zawo.”

4Wokhala mmwamba akuseka;

Ambuye akuwanyoza iwowo.

5Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake

ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,

6“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga

pa Ziyoni, phiri langa loyera.”

7Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula:

Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga;

lero Ine ndakhala Atate ako.

8Tandipempha,

ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako;

malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.

9Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo;

udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”

10Kotero, inu mafumu, chenjerani;

chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.

11Tumikirani Yehova mwa mantha

ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.

12Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye;

kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu,

pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa.

Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help